Add parallel Print Page Options

Mawu a Bilidadi

18 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?
    Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe
    ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,
    kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?
    Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;
    malawi a moto wake sakuwalanso.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;
    nyale ya pambali pake yazima.
Mayendedwe ake amgugu azilala;
    fundo zake zomwe zamugwetsa.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde
    ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Msampha wamkola mwendo;
    khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Amutchera msampha pansi mobisika;
    atchera diwa pa njira yake.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,
    zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,
    tsoka likumudikira.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;
    miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,
    ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;
    awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Mizu yake ikuwuma pansi
    ndipo nthambi zake zikufota
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;
    sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,
    ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,
    kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;
    anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;
    amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

Bildad

18 Then Bildad the Shuhite(A) replied:

“When will you end these speeches?(B)
    Be sensible, and then we can talk.
Why are we regarded as cattle(C)
    and considered stupid in your sight?(D)
You who tear yourself(E) to pieces in your anger,(F)
    is the earth to be abandoned for your sake?
    Or must the rocks be moved from their place?(G)

“The lamp of a wicked man is snuffed out;(H)
    the flame of his fire stops burning.(I)
The light in his tent(J) becomes dark;(K)
    the lamp beside him goes out.(L)
The vigor(M) of his step is weakened;(N)
    his own schemes(O) throw him down.(P)
His feet thrust him into a net;(Q)
    he wanders into its mesh.
A trap seizes him by the heel;
    a snare(R) holds him fast.(S)
10 A noose(T) is hidden for him on the ground;
    a trap(U) lies in his path.(V)
11 Terrors(W) startle him on every side(X)
    and dog(Y) his every step.
12 Calamity(Z) is hungry(AA) for him;
    disaster(AB) is ready for him when he falls.(AC)
13 It eats away parts of his skin;(AD)
    death’s firstborn devours his limbs.(AE)
14 He is torn from the security of his tent(AF)
    and marched off to the king(AG) of terrors.(AH)
15 Fire resides[a] in his tent;(AI)
    burning sulfur(AJ) is scattered over his dwelling.
16 His roots dry up below(AK)
    and his branches wither above.(AL)
17 The memory of him perishes from the earth;(AM)
    he has no name(AN) in the land.(AO)
18 He is driven from light into the realm of darkness(AP)
    and is banished(AQ) from the world.(AR)
19 He has no offspring(AS) or descendants(AT) among his people,
    no survivor(AU) where once he lived.(AV)
20 People of the west are appalled(AW) at his fate;(AX)
    those of the east are seized with horror.
21 Surely such is the dwelling(AY) of an evil man;(AZ)
    such is the place(BA) of one who does not know God.”(BB)

Footnotes

  1. Job 18:15 Or Nothing he had remains