Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

26 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu!
    Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru!
    Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa?
    Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?

“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi,
    ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu;
    chiwonongeko ndi chosaphimbidwa.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho;
    Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,
    koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Iye amaphimba mwezi wowala,
    amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,
    kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera,
    ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja;
    ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga,
    dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake;
    tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona!
    Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

Job

26 Then Job replied:

“How you have helped the powerless!(A)
    How you have saved the arm that is feeble!(B)
What advice you have offered to one without wisdom!
    And what great insight(C) you have displayed!
Who has helped you utter these words?
    And whose spirit spoke from your mouth?(D)

“The dead are in deep anguish,(E)
    those beneath the waters and all that live in them.
The realm of the dead(F) is naked before God;
    Destruction[a](G) lies uncovered.(H)
He spreads out the northern skies(I) over empty space;
    he suspends the earth over nothing.(J)
He wraps up the waters(K) in his clouds,(L)
    yet the clouds do not burst under their weight.
He covers the face of the full moon,
    spreading his clouds(M) over it.
10 He marks out the horizon on the face of the waters(N)
    for a boundary between light and darkness.(O)
11 The pillars of the heavens quake,(P)
    aghast at his rebuke.
12 By his power he churned up the sea;(Q)
    by his wisdom(R) he cut Rahab(S) to pieces.
13 By his breath the skies(T) became fair;
    his hand pierced the gliding serpent.(U)
14 And these are but the outer fringe of his works;
    how faint the whisper(V) we hear of him!(W)
    Who then can understand the thunder of his power?”(X)

Footnotes

  1. Job 26:6 Hebrew Abaddon