Add parallel Print Page Options

27 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,
    Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,
    mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,
    lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;
    mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;
    chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.

“Mdani wanga akhale ngati woyipa,
    wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,
    pamene Mulungu achotsa moyo wake?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake
    pamene zovuta zamugwera?
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?
    Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?

11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo
    sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi.
    Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?

13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,
    cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo
    zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,
    ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,
    ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,
    ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,
    ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;
    akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;
    mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo
    imamuchotsa pamalo pake.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,
    pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu
    ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

Job’s Final Word to His Friends

27 And Job continued his discourse:(A)

“As surely as God lives, who has denied me justice,(B)
    the Almighty,(C) who has made my life bitter,(D)
as long as I have life within me,
    the breath of God(E) in my nostrils,
my lips will not say anything wicked,
    and my tongue will not utter lies.(F)
I will never admit you are in the right;
    till I die, I will not deny my integrity.(G)
I will maintain my innocence(H) and never let go of it;
    my conscience(I) will not reproach me as long as I live.(J)

“May my enemy be like the wicked,(K)
    my adversary(L) like the unjust!
For what hope have the godless(M) when they are cut off,
    when God takes away their life?(N)
Does God listen to their cry
    when distress comes upon them?(O)
10 Will they find delight in the Almighty?(P)
    Will they call on God at all times?

11 “I will teach you about the power of God;
    the ways(Q) of the Almighty I will not conceal.(R)
12 You have all seen this yourselves.
    Why then this meaningless talk?

13 “Here is the fate God allots to the wicked,
    the heritage a ruthless man receives from the Almighty:(S)
14 However many his children,(T) their fate is the sword;(U)
    his offspring will never have enough to eat.(V)
15 The plague will bury those who survive him,
    and their widows will not weep for them.(W)
16 Though he heaps up silver like dust(X)
    and clothes like piles of clay,(Y)
17 what he lays up(Z) the righteous will wear,(AA)
    and the innocent will divide his silver.(AB)
18 The house(AC) he builds is like a moth’s cocoon,(AD)
    like a hut(AE) made by a watchman.
19 He lies down wealthy, but will do so no more;(AF)
    when he opens his eyes, all is gone.(AG)
20 Terrors(AH) overtake him like a flood;(AI)
    a tempest snatches him away in the night.(AJ)
21 The east wind(AK) carries him off, and he is gone;(AL)
    it sweeps him out of his place.(AM)
22 It hurls itself against him without mercy(AN)
    as he flees headlong(AO) from its power.(AP)
23 It claps its hands(AQ) in derision
    and hisses him out of his place.”(AR)