Yobu 28
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
28 Pali mgodi wa siliva
ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Chitsulo amachikumba pansi,
ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale,
amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo,
kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu,
kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko;
iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya,
kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake,
ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi,
palibe kamtema amene anayiona.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo,
ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba,
ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo;
ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso,
motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti?
Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo;
nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’
Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri,
mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri,
kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi,
sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe;
mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi;
nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti?
Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse,
ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti,
‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko,
ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi
ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake,
nayeza kuzama kwa nyanja,
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa
ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake;
nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu,
‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo
ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’ ”
Job 28
New International Version
Interlude: Where Wisdom Is Found
28 There is a mine for silver
and a place where gold is refined.(A)
2 Iron is taken from the earth,
and copper is smelted from ore.(B)
3 Mortals put an end to the darkness;(C)
they search out the farthest recesses
for ore in the blackest darkness.(D)
4 Far from human dwellings they cut a shaft,(E)
in places untouched by human feet;
far from other people they dangle and sway.
5 The earth, from which food comes,(F)
is transformed below as by fire;
6 lapis lazuli(G) comes from its rocks,
and its dust contains nuggets of gold.(H)
7 No bird of prey knows that hidden path,
no falcon’s eye has seen it.(I)
8 Proud beasts(J) do not set foot on it,
and no lion prowls there.(K)
9 People assault the flinty rock(L) with their hands
and lay bare the roots of the mountains.(M)
10 They tunnel through the rock;(N)
their eyes see all its treasures.(O)
11 They search[a] the sources of the rivers(P)
and bring hidden things(Q) to light.
12 But where can wisdom be found?(R)
Where does understanding dwell?(S)
13 No mortal comprehends its worth;(T)
it cannot be found in the land of the living.(U)
14 The deep(V) says, “It is not in me”;
the sea(W) says, “It is not with me.”
15 It cannot be bought with the finest gold,
nor can its price be weighed out in silver.(X)
16 It cannot be bought with the gold of Ophir,(Y)
with precious onyx or lapis lazuli.(Z)
17 Neither gold nor crystal can compare with it,(AA)
nor can it be had for jewels of gold.(AB)
18 Coral(AC) and jasper(AD) are not worthy of mention;
the price of wisdom is beyond rubies.(AE)
19 The topaz(AF) of Cush(AG) cannot compare with it;
it cannot be bought with pure gold.(AH)
20 Where then does wisdom come from?
Where does understanding dwell?(AI)
21 It is hidden from the eyes of every living thing,
concealed even from the birds in the sky.(AJ)
22 Destruction[b](AK) and Death(AL) say,
“Only a rumor of it has reached our ears.”
23 God understands the way to it
and he alone(AM) knows where it dwells,(AN)
24 for he views the ends of the earth(AO)
and sees everything under the heavens.(AP)
25 When he established the force of the wind
and measured out the waters,(AQ)
26 when he made a decree for the rain(AR)
and a path for the thunderstorm,(AS)
27 then he looked at wisdom and appraised it;
he confirmed it and tested it.(AT)
28 And he said to the human race,
“The fear of the Lord—that is wisdom,
and to shun evil(AU) is understanding.”(AV)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.