Add parallel Print Page Options

35 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?
    Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,
    ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu
    pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone
    mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?
    Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?
    Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,
    ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;
    akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,
    amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi
    ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye
    chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;
    Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti
    Iye saona zimene zikuchitika.
Iye adzaweruza molungama ngati
    inu mutamudikira
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,
    zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,
    mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

35 Then Elihu said:

“Do you think this is just?
    You say, ‘I am in the right,(A) not God.’(B)
Yet you ask him, ‘What profit is it to me,[a]
    and what do I gain by not sinning?’(C)

“I would like to reply to you
    and to your friends with you.
Look up at the heavens(D) and see;
    gaze at the clouds so high above you.(E)
If you sin, how does that affect him?
    If your sins are many, what does that do to him?(F)
If you are righteous, what do you give to him,(G)
    or what does he receive(H) from your hand?(I)
Your wickedness only affects humans like yourself,(J)
    and your righteousness only other people.(K)

“People cry out(L) under a load of oppression;(M)
    they plead for relief from the arm of the powerful.(N)
10 But no one says, ‘Where is God my Maker,(O)
    who gives songs(P) in the night,(Q)
11 who teaches(R) us(S) more than he teaches[b] the beasts of the earth
    and makes us wiser than[c] the birds in the sky?’
12 He does not answer(T) when people cry out
    because of the arrogance(U) of the wicked.(V)
13 Indeed, God does not listen to their empty plea;
    the Almighty pays no attention to it.(W)
14 How much less, then, will he listen
    when you say that you do not see him,(X)
that your case(Y) is before him
    and you must wait for him,(Z)
15 and further, that his anger never punishes(AA)
    and he does not take the least notice of wickedness.[d](AB)
16 So Job opens his mouth with empty talk;(AC)
    without knowledge he multiplies words.”(AD)

Footnotes

  1. Job 35:3 Or you
  2. Job 35:11 Or night, / 11 who teaches us by
  3. Job 35:11 Or us wise by
  4. Job 35:15 Symmachus, Theodotion and Vulgate; the meaning of the Hebrew for this word is uncertain.