Add parallel Print Page Options

39 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?
    Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?
    Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;
    pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;
    kenaka amachoka ndipo sabwereranso.

“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?
    Ndani amamasula zingwe zake?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,
    nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;
    ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu
    ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.

“Kodi njati ingavomere kukutumikira?
    Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?
    Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?
    Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako
    ndi kumuyika ku malo opunthira?

13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,
    koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi
    ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,
    ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;
    Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,
    simvetsa kanthu kalikonse.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,
    imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.

19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo
    kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,
    ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,
    ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse;
    sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake
    pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;
    satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’
    Amamva fungo la nkhondo ali patali,
    kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.

26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,
    ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka
    ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;
    chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;
    maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ana ake amayamwa magazi,
    ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

39 “Do you know when the mountain goats(A) give birth?
    Do you watch when the doe bears her fawn?(B)
Do you count the months till they bear?
    Do you know the time they give birth?(C)
They crouch down and bring forth their young;
    their labor pains are ended.
Their young thrive and grow strong in the wilds;
    they leave and do not return.

“Who let the wild donkey(D) go free?
    Who untied its ropes?
I gave it the wasteland(E) as its home,
    the salt flats(F) as its habitat.(G)
It laughs(H) at the commotion in the town;
    it does not hear a driver’s shout.(I)
It ranges the hills(J) for its pasture
    and searches for any green thing.

“Will the wild ox(K) consent to serve you?(L)
    Will it stay by your manger(M) at night?
10 Can you hold it to the furrow with a harness?(N)
    Will it till the valleys behind you?
11 Will you rely on it for its great strength?(O)
    Will you leave your heavy work to it?
12 Can you trust it to haul in your grain
    and bring it to your threshing floor?

13 “The wings of the ostrich flap joyfully,
    though they cannot compare
    with the wings and feathers of the stork.(P)
14 She lays her eggs on the ground
    and lets them warm in the sand,
15 unmindful that a foot may crush them,
    that some wild animal may trample them.(Q)
16 She treats her young harshly,(R) as if they were not hers;
    she cares not that her labor was in vain,
17 for God did not endow her with wisdom
    or give her a share of good sense.(S)
18 Yet when she spreads her feathers to run,
    she laughs(T) at horse and rider.

19 “Do you give the horse its strength(U)
    or clothe its neck with a flowing mane?
20 Do you make it leap like a locust,(V)
    striking terror(W) with its proud snorting?(X)
21 It paws fiercely, rejoicing in its strength,(Y)
    and charges into the fray.(Z)
22 It laughs(AA) at fear, afraid of nothing;
    it does not shy away from the sword.
23 The quiver(AB) rattles against its side,
    along with the flashing spear(AC) and lance.
24 In frenzied excitement it eats up the ground;
    it cannot stand still when the trumpet sounds.(AD)
25 At the blast of the trumpet(AE) it snorts, ‘Aha!’
    It catches the scent of battle from afar,
    the shout of commanders and the battle cry.(AF)

26 “Does the hawk take flight by your wisdom
    and spread its wings toward the south?(AG)
27 Does the eagle soar at your command
    and build its nest on high?(AH)
28 It dwells on a cliff and stays there at night;
    a rocky crag(AI) is its stronghold.
29 From there it looks for food;(AJ)
    its eyes detect it from afar.
30 Its young ones feast on blood,
    and where the slain are, there it is.”(AK)