Add parallel Print Page Options

Mawu a Elifazi

Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?
    Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,
    momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;
    unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,
    zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?
    Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?
    Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,
    ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;
    amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Mikango imabangula ndi kulira,
    komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,
    ndipo ana amkango amamwazikana.

12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri,
    makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,
    nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera
    ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,
    ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Chinthucho chinayimirira
    koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.
Chinthu chinayima patsogolo panga,
    kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?
    Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,
    ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,
    amene maziko awo ndi fumbi,
    amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;
    mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,
    kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Eliphaz

Then Eliphaz the Temanite(A) replied:

“If someone ventures a word with you, will you be impatient?
    But who can keep from speaking?(B)
Think how you have instructed many,(C)
    how you have strengthened feeble hands.(D)
Your words have supported those who stumbled;(E)
    you have strengthened faltering knees.(F)
But now trouble comes to you, and you are discouraged;(G)
    it strikes(H) you, and you are dismayed.(I)
Should not your piety be your confidence(J)
    and your blameless(K) ways your hope?

“Consider now: Who, being innocent, has ever perished?(L)
    Where were the upright ever destroyed?(M)
As I have observed,(N) those who plow evil(O)
    and those who sow trouble reap it.(P)
At the breath of God(Q) they perish;
    at the blast of his anger they are no more.(R)
10 The lions may roar(S) and growl,
    yet the teeth of the great lions(T) are broken.(U)
11 The lion perishes for lack of prey,(V)
    and the cubs of the lioness are scattered.(W)

12 “A word(X) was secretly brought to me,
    my ears caught a whisper(Y) of it.(Z)
13 Amid disquieting dreams in the night,
    when deep sleep falls on people,(AA)
14 fear and trembling(AB) seized me
    and made all my bones shake.(AC)
15 A spirit glided past my face,
    and the hair on my body stood on end.(AD)
16 It stopped,
    but I could not tell what it was.
A form stood before my eyes,
    and I heard a hushed voice:(AE)
17 ‘Can a mortal be more righteous than God?(AF)
    Can even a strong man be more pure than his Maker?(AG)
18 If God places no trust in his servants,(AH)
    if he charges his angels with error,(AI)
19 how much more those who live in houses of clay,(AJ)
    whose foundations(AK) are in the dust,(AL)
    who are crushed(AM) more readily than a moth!(AN)
20 Between dawn and dusk they are broken to pieces;
    unnoticed, they perish forever.(AO)
21 Are not the cords of their tent pulled up,(AP)
    so that they die(AQ) without wisdom?’(AR)