Add parallel Print Page Options

Yobu

42 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,

“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse;
    chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru?
    Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse,
    zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.

“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula;
    ndidzakufunsa
    ndipo iwe udzandiyankhe.’
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga,
    koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi,
    ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”

Mulungu Adalitsa Yobu

Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu. Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.” Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.

10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale. 11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.

12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000. 13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu. 14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki. 15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.

16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi. 17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.

Job

42 Then Job replied to the Lord:

“I know that you can do all things;(A)
    no purpose of yours can be thwarted.(B)
You asked, ‘Who is this that obscures my plans without knowledge?’(C)
    Surely I spoke of things I did not understand,
    things too wonderful for me to know.(D)

“You said, ‘Listen now, and I will speak;
    I will question you,
    and you shall answer me.’(E)
My ears had heard of you(F)
    but now my eyes have seen you.(G)
Therefore I despise myself(H)
    and repent(I) in dust and ashes.”(J)

Epilogue

After the Lord had said these things to Job(K), he said to Eliphaz the Temanite, “I am angry with you and your two friends,(L) because you have not spoken the truth about me, as my servant Job has.(M) So now take seven bulls and seven rams(N) and go to my servant Job(O) and sacrifice a burnt offering(P) for yourselves. My servant Job will pray for you, and I will accept his prayer(Q) and not deal with you according to your folly.(R) You have not spoken the truth about me, as my servant Job has.”(S) So Eliphaz the Temanite, Bildad the Shuhite and Zophar the Naamathite(T) did what the Lord told them; and the Lord accepted Job’s prayer.(U)

10 After Job had prayed for his friends, the Lord restored his fortunes(V) and gave him twice as much as he had before.(W) 11 All his brothers and sisters and everyone who had known him before(X) came and ate with him in his house. They comforted and consoled him over all the trouble the Lord had brought on him,(Y) and each one gave him a piece of silver[a] and a gold ring.

12 The Lord blessed the latter part of Job’s life more than the former part. He had fourteen thousand sheep, six thousand camels, a thousand yoke of oxen and a thousand donkeys. 13 And he also had seven sons and three daughters. 14 The first daughter he named Jemimah, the second Keziah and the third Keren-Happuch. 15 Nowhere in all the land were there found women as beautiful as Job’s daughters, and their father granted them an inheritance along with their brothers.

16 After this, Job lived a hundred and forty years; he saw his children and their children to the fourth generation. 17 And so Job died, an old man and full of years.(Z)

Footnotes

  1. Job 42:11 Hebrew him a kesitah; a kesitah was a unit of money of unknown weight and value.