Add parallel Print Page Options

“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?
    Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,
    kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,
    ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’
    Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,
    khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,
    ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;
    sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Amene akundiona tsopano akundiona;
    mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,
    momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake
    ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;
    ndidzayankhula mopsinjika mtima,
    ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja
    kuti inu mundiyikire alonda?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga
    ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto
    ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,
    kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.
    Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,
    kuti muzisamala zochita zake,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse
    ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda
    kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,
    Inu wopenyetsetsa anthu?
Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?
    Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga
    ndi kundichotsera machimo anga?
Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;
    mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

“Do not mortals have hard service(A) on earth?(B)
    Are not their days like those of hired laborers?(C)
Like a slave longing for the evening shadows,(D)
    or a hired laborer waiting to be paid,(E)
so I have been allotted months of futility,
    and nights of misery have been assigned to me.(F)
When I lie down I think, ‘How long before I get up?’(G)
    The night drags on, and I toss and turn until dawn.(H)
My body is clothed with worms(I) and scabs,
    my skin is broken and festering.(J)

“My days are swifter than a weaver’s shuttle,(K)
    and they come to an end without hope.(L)
Remember, O God, that my life is but a breath;(M)
    my eyes will never see happiness again.(N)
The eye that now sees me will see me no longer;
    you will look for me, but I will be no more.(O)
As a cloud vanishes(P) and is gone,
    so one who goes down to the grave(Q) does not return.(R)
10 He will never come to his house again;
    his place(S) will know him no more.(T)

11 “Therefore I will not keep silent;(U)
    I will speak out in the anguish(V) of my spirit,
    I will complain(W) in the bitterness of my soul.(X)
12 Am I the sea,(Y) or the monster of the deep,(Z)
    that you put me under guard?(AA)
13 When I think my bed will comfort me
    and my couch will ease my complaint,(AB)
14 even then you frighten me with dreams
    and terrify(AC) me with visions,(AD)
15 so that I prefer strangling and death,(AE)
    rather than this body of mine.(AF)
16 I despise my life;(AG) I would not live forever.(AH)
    Let me alone;(AI) my days have no meaning.(AJ)

17 “What is mankind that you make so much of them,
    that you give them so much attention,(AK)
18 that you examine them every morning(AL)
    and test them(AM) every moment?(AN)
19 Will you never look away from me,(AO)
    or let me alone even for an instant?(AP)
20 If I have sinned, what have I done to you,(AQ)
    you who see everything we do?
Why have you made me your target?(AR)
    Have I become a burden to you?[a](AS)
21 Why do you not pardon my offenses
    and forgive my sins?(AT)
For I will soon lie down in the dust;(AU)
    you will search for me, but I will be no more.”(AV)

Footnotes

  1. Job 7:20 A few manuscripts of the Masoretic Text, an ancient Hebrew scribal tradition and Septuagint; most manuscripts of the Masoretic Text I have become a burden to myself.