Yobu 9
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mawu a Yobu
9 Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.
Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,
Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.
Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,
ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake
ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;
Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba
ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,
nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;
akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?
Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake;
ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?
Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;
ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,
sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,
ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso
koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!
Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;
ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa,
sindidziyenereza ndekha;
moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,
‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,
Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa
Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.
Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;
masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,
ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,
ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 ndikuopabe mavuto anga onse,
popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa
ndivutikirenji popanda phindu?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri
ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 mutha kundiponyabe pa dzala,
kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,
sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,
kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine
kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,
koma monga zililimu, sindingathe.
Job 9
New International Version
Job
9 Then Job replied:
2 “Indeed, I know that this is true.
But how can mere mortals prove their innocence before God?(A)
3 Though they wished to dispute with him,(B)
they could not answer him one time out of a thousand.(C)
4 His wisdom(D) is profound, his power is vast.(E)
Who has resisted(F) him and come out unscathed?(G)
5 He moves mountains(H) without their knowing it
and overturns them in his anger.(I)
6 He shakes the earth(J) from its place
and makes its pillars tremble.(K)
7 He speaks to the sun and it does not shine;(L)
he seals off the light of the stars.(M)
8 He alone stretches out the heavens(N)
and treads on the waves of the sea.(O)
9 He is the Maker(P) of the Bear[a] and Orion,
the Pleiades and the constellations of the south.(Q)
10 He performs wonders(R) that cannot be fathomed,
miracles that cannot be counted.(S)
11 When he passes me, I cannot see him;
when he goes by, I cannot perceive him.(T)
12 If he snatches away, who can stop him?(U)
Who can say to him, ‘What are you doing?’(V)
13 God does not restrain his anger;(W)
even the cohorts of Rahab(X) cowered at his feet.
14 “How then can I dispute with him?
How can I find words to argue with him?(Y)
15 Though I were innocent, I could not answer him;(Z)
I could only plead(AA) with my Judge(AB) for mercy.(AC)
16 Even if I summoned him and he responded,
I do not believe he would give me a hearing.(AD)
17 He would crush me(AE) with a storm(AF)
and multiply(AG) my wounds for no reason.(AH)
18 He would not let me catch my breath
but would overwhelm me with misery.(AI)
19 If it is a matter of strength, he is mighty!(AJ)
And if it is a matter of justice, who can challenge him[b]?(AK)
20 Even if I were innocent, my mouth would condemn me;
if I were blameless, it would pronounce me guilty.(AL)
21 “Although I am blameless,(AM)
I have no concern for myself;(AN)
I despise my own life.(AO)
22 It is all the same; that is why I say,
‘He destroys both the blameless and the wicked.’(AP)
23 When a scourge(AQ) brings sudden death,
he mocks the despair of the innocent.(AR)
24 When a land falls into the hands of the wicked,(AS)
he blindfolds its judges.(AT)
If it is not he, then who is it?(AU)
25 “My days are swifter than a runner;(AV)
they fly away without a glimpse of joy.(AW)
26 They skim past(AX) like boats of papyrus,(AY)
like eagles swooping down on their prey.(AZ)
27 If I say, ‘I will forget my complaint,(BA)
I will change my expression, and smile,’
28 I still dread(BB) all my sufferings,
for I know you will not hold me innocent.(BC)
29 Since I am already found guilty,
why should I struggle in vain?(BD)
30 Even if I washed myself with soap(BE)
and my hands(BF) with cleansing powder,(BG)
31 you would plunge me into a slime pit(BH)
so that even my clothes would detest me.(BI)
32 “He is not a mere mortal(BJ) like me that I might answer him,(BK)
that we might confront each other in court.(BL)
33 If only there were someone to mediate between us,(BM)
someone to bring us together,(BN)
34 someone to remove God’s rod from me,(BO)
so that his terror would frighten me no more.(BP)
35 Then I would speak up without fear of him,(BQ)
but as it now stands with me, I cannot.(BR)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.