Add parallel Print Page Options

“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?
    Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,
    kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,
    ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’
    Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,
    khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,
    ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;
    sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Amene akundiona tsopano akundiona;
    mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,
    momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake
    ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;
    ndidzayankhula mopsinjika mtima,
    ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja
    kuti inu mundiyikire alonda?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga
    ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto
    ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,
    kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.
    Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,
    kuti muzisamala zochita zake,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse
    ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda
    kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,
    Inu wopenyetsetsa anthu?
Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?
    Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga
    ndi kundichotsera machimo anga?
Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;
    mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”