Yoswa 12
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mayina a Mafumu Ogonjetsedwa
12 Aisraeli anagonjetsa dziko lonse la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku chigwa cha Arinoni mpaka ku phiri la Herimoni pamodzi ndi dera lonse la kummawa kwa Araba. Iwo anatenga dzikoli kukhala lawo, ndipo mafumu a dzikoli anali awa:
2 Sihoni mfumu ya Aamori,
amene ankakhala mu Hesiboni. Iye analamulira kuyambira ku Aroeri mzinda umene uli mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni, mpaka ku mtsinje wa Yaboki, umene uli mʼmalire mwa Aamori, kuphatikizanso theka la dziko la Giliyadi. 3 Iye ankalamuliranso dera la chigwa cha Yorodani kuyambira ku Nyanja ya Kinereti, kummawa ndi kumatsika mpaka ku Beti-Yesimoti, mzinda umene unali kummawa kwa Nyanja ya Mchere ndi kutsikabe kummwera mpaka pa tsinde pa phiri la Pisiga.
4 Ogi mfumu ya mzinda wa Basani,
amene anali mmodzi mwa otsala mwa Arefaimu. Iye ankakhala ku Asiteroti ndi Ederi. 5 Dera la ufumu wake linafika ku phiri la Herimoni, ku Saleka ndi dziko lonse la Basani mpaka ku malire ndi anthu a ku Gesuri Makati. Ufumu wake unaphatikizanso theka la Giliyadi mpaka ku malire a mfumu Sihoni ya ku Hesiboni.
6 Mose mtumiki wa Yehova ndi Aisraeli anawagonjetsa ndipo anapereka dziko lawo kwa anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti chikhale cholowa chawo.
7 Yoswa ndi Aisraeli onse anagonjetsa mafumu onse okhala kumadzulo kwa mtsinje wa Yorodani kuyambira ku Baala-Gadi, ku chigwa cha Lebanoni mpaka ku phiri la Halaki, kumapita cha ku Seiri. Yoswa anagawira dzikolo mafuko a Israeli kuti likhale cholowa chawo. 8 Dziko limeneli linali dera la ku mapiri, chigwa cha kumadzulo, chigwa cha Yorodani, ku matsitso a kummawa, ndi dziko la chipululu la kummwera. Amene ankakhala mʼdzikoli anali Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. Mafumu ake anali awa:
9 mfumu ya Yeriko | imodzi |
mfumu ya Ai (kufupi ndi Beteli | imodzi |
10 mfumu ya Yerusalemu | imodzi |
mfumu ya Hebroni | imodzi |
11 mfumu ya Yarimuti | imodzi |
mfumu ya Lakisi | imodzi |
12 mfumu ya Egiloni | imodzi |
mfumu ya Gezeri | imodzi |
13 mfumu ya Debri | imodzi |
mfumu ya Gederi | imodzi |
14 mfumu ya Horima | imodzi |
mfumu ya Aradi | imodzi |
15 mfumu ya Libina | imodzi |
mfumu ya Adulamu | imodzi |
16 mfumu ya Makeda | imodzi |
mfumu ya Beteli | imodzi |
17 mfumu ya Tapuwa | imodzi |
mfumu ya Heferi | imodzi |
18 mfumu ya Afeki | imodzi |
mfumu ya Lasaroni | imodzi |
19 mfumu ya Madoni | imodzi |
mfumu ya Hazori | imodzi |
20 mfumu ya Simuroni Meroni | imodzi |
mfumu ya Akisafu | imodzi |
21 mfumu ya Taanaki | imodzi |
mfumu ya Megido | imodzi |
22 mfumu ya Kadesi | imodzi |
mfumu ya Yokineamu ku Karimeli | imodzi |
23 mfumu ya Dori ku Nafoti Dori | imodzi |
mfumu ya Goyini ku Giligala | imodzi |
24 mfumu ya Tiriza | imodzi |
mafumu onse pamodzi analipo 31. |
Joshua 12
New International Version
List of Defeated Kings
12 These are the kings of the land whom the Israelites had defeated and whose territory they took(A) over east of the Jordan,(B) from the Arnon(C) Gorge to Mount Hermon,(D) including all the eastern side of the Arabah:(E)
2 Sihon king of the Amorites, who reigned in Heshbon.(F)
He ruled from Aroer(G) on the rim of the Arnon Gorge—from the middle of the gorge—to the Jabbok River,(H) which is the border of the Ammonites.(I) This included half of Gilead.(J) 3 He also ruled over the eastern Arabah from the Sea of Galilee[a](K) to the Sea of the Arabah (that is, the Dead Sea(L)), to Beth Jeshimoth,(M) and then southward below the slopes of Pisgah.(N)
4 And the territory of Og king of Bashan,(O) one of the last of the Rephaites,(P) who reigned in Ashtaroth(Q) and Edrei.
5 He ruled over Mount Hermon, Salekah,(R) all of Bashan(S) to the border of the people of Geshur(T) and Maakah,(U) and half of Gilead(V) to the border of Sihon king of Heshbon.
6 Moses, the servant of the Lord, and the Israelites conquered them.(W) And Moses the servant of the Lord gave their land to the Reubenites, the Gadites and the half-tribe of Manasseh to be their possession.(X)
7 Here is a list of the kings of the land that Joshua and the Israelites conquered on the west side of the Jordan, from Baal Gad in the Valley of Lebanon(Y) to Mount Halak, which rises toward Seir. Joshua gave their lands as an inheritance to the tribes of Israel according to their tribal divisions. 8 The lands included the hill country, the western foothills, the Arabah, the mountain slopes, the wilderness and the Negev.(Z) These were the lands of the Hittites, Amorites, Canaanites, Perizzites, Hivites and Jebusites. These were the kings:(AA)
9 the king of Jericho(AB) | one |
the king of Ai(AC) (near Bethel(AD)) | one |
10 the king of Jerusalem(AE) | one |
the king of Hebron | one |
11 the king of Jarmuth | one |
the king of Lachish(AF) | one |
12 the king of Eglon(AG) | one |
the king of Gezer(AH) | one |
13 the king of Debir(AI) | one |
the king of Geder | one |
14 the king of Hormah(AJ) | one |
the king of Arad(AK) | one |
15 the king of Libnah(AL) | one |
the king of Adullam(AM) | one |
16 the king of Makkedah(AN) | one |
the king of Bethel(AO) | one |
17 the king of Tappuah(AP) | one |
the king of Hepher(AQ) | one |
18 the king of Aphek(AR) | one |
the king of Lasharon | one |
19 the king of Madon | one |
the king of Hazor(AS) | one |
20 the king of Shimron Meron | one |
the king of Akshaph(AT) | one |
21 the king of Taanach(AU) | one |
the king of Megiddo(AV) | one |
22 the king of Kedesh(AW) | one |
the king of Jokneam(AX) in Carmel(AY) | one |
23 the king of Dor (in Naphoth Dor(AZ)) | one |
the king of Goyim in Gilgal | one |
24 the king of Tirzah(BA) | one |
thirty-one kings in all.(BB) |
Footnotes
- Joshua 12:3 Hebrew Kinnereth
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.