Add parallel Print Page Options

Mayiko Otsala Oyenera Kulandidwa

13 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.

“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto. Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori. Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.

“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira. Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”

Kugawidwa kwa Dziko la Kummawa kwa Yorodani

Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.

Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni. 10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni. 11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka. 12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali. 13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.

14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.

15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.

16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba. 17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni, 18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati. 19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa, 20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti. 21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni. 22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga. 23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.

24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:

25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba; 26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri. 27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto. 28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.

29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.

30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko. 31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.

32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani. 33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

Land Still to Be Taken

13 When Joshua had grown old,(A) the Lord said to him, “You are now very old, and there are still very large areas of land to be taken over.

“This is the land that remains: all the regions of the Philistines(B) and Geshurites,(C) from the Shihor River(D) on the east of Egypt to the territory of Ekron(E) on the north, all of it counted as Canaanite though held by the five Philistine rulers(F) in Gaza, Ashdod,(G) Ashkelon,(H) Gath and Ekron; the territory of the Avvites(I) on the south; all the land of the Canaanites, from Arah of the Sidonians as far as Aphek(J) and the border of the Amorites;(K) the area of Byblos;(L) and all Lebanon(M) to the east, from Baal Gad below Mount Hermon(N) to Lebo Hamath.(O)

“As for all the inhabitants of the mountain regions from Lebanon to Misrephoth Maim,(P) that is, all the Sidonians, I myself will drive them out(Q) before the Israelites. Be sure to allocate this land to Israel for an inheritance, as I have instructed you,(R) and divide it as an inheritance(S) among the nine tribes and half of the tribe of Manasseh.”

Division of the Land East of the Jordan

The other half of Manasseh,[a] the Reubenites and the Gadites had received the inheritance that Moses had given them east of the Jordan, as he, the servant of the Lord, had assigned(T) it to them.(U)

It extended from Aroer(V) on the rim of the Arnon Gorge, and from the town in the middle of the gorge, and included the whole plateau(W) of Medeba as far as Dibon,(X) 10 and all the towns of Sihon king of the Amorites, who ruled in Heshbon,(Y) out to the border of the Ammonites.(Z) 11 It also included Gilead,(AA) the territory of the people of Geshur and Maakah, all of Mount Hermon and all Bashan as far as Salekah(AB) 12 that is, the whole kingdom of Og in Bashan,(AC) who had reigned in Ashtaroth(AD) and Edrei.(AE) (He was the last of the Rephaites.(AF)) Moses had defeated them and taken over their land.(AG) 13 But the Israelites did not drive out the people of Geshur(AH) and Maakah,(AI) so they continue to live among the Israelites to this day.(AJ)

14 But to the tribe of Levi he gave no inheritance, since the food offerings presented to the Lord, the God of Israel, are their inheritance, as he promised them.(AK)

15 This is what Moses had given to the tribe of Reuben, according to its clans:

16 The territory from Aroer(AL) on the rim of the Arnon Gorge, and from the town in the middle of the gorge, and the whole plateau past Medeba(AM) 17 to Heshbon and all its towns on the plateau,(AN) including Dibon,(AO) Bamoth Baal,(AP) Beth Baal Meon,(AQ) 18 Jahaz,(AR) Kedemoth,(AS) Mephaath,(AT) 19 Kiriathaim,(AU) Sibmah,(AV) Zereth Shahar on the hill in the valley, 20 Beth Peor,(AW) the slopes of Pisgah, and Beth Jeshimoth— 21 all the towns on the plateau(AX) and the entire realm of Sihon king of the Amorites, who ruled at Heshbon. Moses had defeated him and the Midianite chiefs,(AY) Evi, Rekem, Zur, Hur and Reba(AZ)—princes allied with Sihon—who lived in that country. 22 In addition to those slain in battle, the Israelites had put to the sword Balaam son of Beor,(BA) who practiced divination.(BB) 23 The boundary of the Reubenites was the bank of the Jordan. These towns and their villages were the inheritance of the Reubenites, according to their clans.(BC)

24 This is what Moses had given to the tribe of Gad, according to its clans:

25 The territory of Jazer,(BD) all the towns of Gilead(BE) and half the Ammonite country as far as Aroer, near Rabbah;(BF) 26 and from Heshbon(BG) to Ramath Mizpah and Betonim, and from Mahanaim(BH) to the territory of Debir;(BI) 27 and in the valley, Beth Haram, Beth Nimrah,(BJ) Sukkoth(BK) and Zaphon(BL) with the rest of the realm of Sihon king of Heshbon (the east side of the Jordan, the territory up to the end of the Sea of Galilee[b](BM)). 28 These towns and their villages were the inheritance of the Gadites,(BN) according to their clans.

29 This is what Moses had given to the half-tribe of Manasseh, that is, to half the family of the descendants of Manasseh, according to its clans:

30 The territory extending from Mahanaim(BO) and including all of Bashan,(BP) the entire realm of Og king of Bashan(BQ)—all the settlements of Jair(BR) in Bashan, sixty towns, 31 half of Gilead, and Ashtaroth and Edrei (the royal cities of Og in Bashan).(BS) This was for the descendants of Makir(BT) son of Manasseh—for half of the sons of Makir, according to their clans.(BU)

32 This is the inheritance Moses had given when he was in the plains of Moab(BV) across the Jordan east of Jericho.(BW) 33 But to the tribe of Levi, Moses had given no inheritance;(BX) the Lord, the God of Israel, is their inheritance,(BY) as he promised them.(BZ)

Footnotes

  1. Joshua 13:8 Hebrew With it (that is, with the other half of Manasseh)
  2. Joshua 13:27 Hebrew Kinnereth