Add parallel Print Page Options

Rahabe ndi Anthu Ozonda Dziko

Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.

Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.” Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”

Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera. Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.” Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo. Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.

Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu. 10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu. 11 Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi. 12 Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga. 13 Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”

14 Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”

15 Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe. 16 Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”

17 Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi 18 tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno. 19 Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu. 20 Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”

21 Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.

22 Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza. 23 Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira. 24 Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

Rahab and the Spies

Then Joshua son of Nun secretly sent two spies(A) from Shittim.(B) “Go, look over(C) the land,” he said, “especially Jericho.(D)” So they went and entered the house of a prostitute named Rahab(E) and stayed there.

The king of Jericho was told, “Look, some of the Israelites have come here tonight to spy out the land.” So the king of Jericho sent this message to Rahab:(F) “Bring out the men who came to you and entered your house, because they have come to spy out the whole land.”

But the woman had taken the two men(G) and hidden them.(H) She said, “Yes, the men came to me, but I did not know where they had come from. At dusk, when it was time to close the city gate,(I) they left. I don’t know which way they went. Go after them quickly. You may catch up with them.”(J) (But she had taken them up to the roof and hidden them under the stalks of flax(K) she had laid out on the roof.)(L) So the men set out in pursuit of the spies on the road that leads to the fords of the Jordan,(M) and as soon as the pursuers(N) had gone out, the gate was shut.

Before the spies lay down for the night, she went up on the roof(O) and said to them, “I know that the Lord has given you this land and that a great fear(P) of you has fallen on us, so that all who live in this country are melting in fear because of you. 10 We have heard how the Lord dried up(Q) the water of the Red Sea[a] for you when you came out of Egypt,(R) and what you did to Sihon and Og,(S) the two kings of the Amorites(T) east of the Jordan,(U) whom you completely destroyed.[b](V) 11 When we heard of it, our hearts melted in fear(W) and everyone’s courage failed(X) because of you,(Y) for the Lord your God(Z) is God in heaven above and on the earth(AA) below.

12 “Now then, please swear to me(AB) by the Lord that you will show kindness(AC) to my family, because I have shown kindness to you. Give me a sure sign(AD) 13 that you will spare the lives of my father and mother, my brothers and sisters, and all who belong to them(AE)—and that you will save us from death.”

14 “Our lives for your lives!”(AF) the men assured her. “If you don’t tell what we are doing, we will treat you kindly and faithfully(AG) when the Lord gives us the land.”

15 So she let them down by a rope(AH) through the window,(AI) for the house she lived in was part of the city wall. 16 She said to them, “Go to the hills(AJ) so the pursuers(AK) will not find you. Hide yourselves there three days(AL) until they return, and then go on your way.”(AM)

17 Now the men had said to her, “This oath(AN) you made us swear will not be binding on us 18 unless, when we enter the land, you have tied this scarlet cord(AO) in the window(AP) through which you let us down, and unless you have brought your father and mother, your brothers and all your family(AQ) into your house. 19 If any of them go outside your house into the street, their blood will be on their own heads;(AR) we will not be responsible. As for those who are in the house with you, their blood will be on our head(AS) if a hand is laid on them. 20 But if you tell what we are doing, we will be released from the oath you made us swear.(AT)

21 “Agreed,” she replied. “Let it be as you say.”

So she sent them away, and they departed. And she tied the scarlet cord(AU) in the window.(AV)

22 When they left, they went into the hills and stayed there three days,(AW) until the pursuers(AX) had searched all along the road and returned without finding them. 23 Then the two men started back. They went down out of the hills, forded the river and came to Joshua son of Nun and told him everything that had happened to them. 24 They said to Joshua, “The Lord has surely given the whole land into our hands;(AY) all the people are melting in fear(AZ) because of us.”

Footnotes

  1. Joshua 2:10 Or the Sea of Reeds
  2. Joshua 2:10 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.