Add parallel Print Page Options

Kutsanzika kwa Yoswa

23 Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri. Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri. Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo. Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa. Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.

“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo. Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira. Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.

“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu. 10 Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera. 11 Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.

12 “Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo, 13 pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.

14 “Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe. 15 Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani. 16 Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

Joshua’s Farewell to the Leaders

23 After a long time had passed and the Lord had given Israel rest(A) from all their enemies around them, Joshua, by then a very old man,(B) summoned all Israel—their elders,(C) leaders, judges and officials(D)—and said to them: “I am very old.(E) You yourselves have seen everything the Lord your God has done to all these nations for your sake; it was the Lord your God who fought for you.(F) Remember how I have allotted(G) as an inheritance(H) for your tribes all the land of the nations that remain—the nations I conquered—between the Jordan and the Mediterranean Sea(I) in the west. The Lord your God himself will push them out(J) for your sake. He will drive them out(K) before you, and you will take possession of their land, as the Lord your God promised you.(L)

“Be very strong; be careful to obey all that is written in the Book of the Law(M) of Moses, without turning aside(N) to the right or to the left.(O) Do not associate with these nations that remain among you; do not invoke the names of their gods or swear(P) by them. You must not serve them or bow down(Q) to them. But you are to hold fast to the Lord(R) your God, as you have until now.

“The Lord has driven out before you great and powerful nations;(S) to this day no one has been able to withstand you.(T) 10 One of you routs a thousand,(U) because the Lord your God fights for you,(V) just as he promised. 11 So be very careful(W) to love the Lord(X) your God.

12 “But if you turn away and ally yourselves with the survivors of these nations that remain among you and if you intermarry with them(Y) and associate with them,(Z) 13 then you may be sure that the Lord your God will no longer drive out(AA) these nations before you. Instead, they will become snares(AB) and traps for you, whips on your backs and thorns in your eyes,(AC) until you perish from this good land,(AD) which the Lord your God has given you.

14 “Now I am about to go the way of all the earth.(AE) You know with all your heart and soul that not one of all the good promises the Lord your God gave you has failed. Every promise(AF) has been fulfilled; not one has failed.(AG) 15 But just as all the good things(AH) the Lord your God has promised you have come to you, so he will bring on you all the evil things(AI) he has threatened, until the Lord your God has destroyed you(AJ) from this good land he has given you.(AK) 16 If you violate the covenant of the Lord your God, which he commanded you, and go and serve other gods and bow down to them, the Lord’s anger will burn against you, and you will quickly perish from the good land he has given you.(AL)