Add parallel Print Page Options

Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa, “Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse. Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’ ”

Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse, ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli, kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’ Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’ ”

Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko. Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.

10 Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira. 11 Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova. 12 Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira. 13 Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.

14 Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.

15 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, 16 “Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”

17 Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.

18 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.

19 Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko. 20 Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija. 21 Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’ 22 Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’ 23 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma. 24 Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”

When the whole nation had finished crossing the Jordan,(A) the Lord said to Joshua, “Choose twelve men(B) from among the people, one from each tribe, and tell them to take up twelve stones(C) from the middle of the Jordan,(D) from right where the priests are standing, and carry them over with you and put them down at the place where you stay tonight.(E)

So Joshua called together the twelve men(F) he had appointed from the Israelites, one from each tribe, and said to them, “Go over before the ark of the Lord your God into the middle of the Jordan.(G) Each of you is to take up a stone on his shoulder, according to the number of the tribes of the Israelites, to serve as a sign(H) among you. In the future, when your children(I) ask you, ‘What do these stones mean?’(J) tell them that the flow of the Jordan was cut off(K) before the ark of the covenant of the Lord. When it crossed the Jordan, the waters of the Jordan were cut off. These stones are to be a memorial(L) to the people of Israel forever.”

So the Israelites did as Joshua commanded them. They took twelve stones(M) from the middle of the Jordan,(N) according to the number of the tribes of the Israelites, as the Lord had told Joshua;(O) and they carried them over with them to their camp, where they put them down. Joshua set up the twelve stones(P) that had been[a] in the middle of the Jordan at the spot where the priests who carried the ark of the covenant had stood. And they are there to this day.(Q)

10 Now the priests who carried the ark remained standing in the middle of the Jordan until everything the Lord had commanded Joshua was done by the people, just as Moses had directed Joshua. The people hurried over, 11 and as soon as all of them had crossed, the ark of the Lord and the priests came to the other side while the people watched. 12 The men of Reuben,(R) Gad(S) and the half-tribe of Manasseh(T) crossed over, ready for battle, in front of the Israelites,(U) as Moses had directed them.(V) 13 About forty thousand armed for battle(W) crossed over(X) before the Lord to the plains of Jericho for war.

14 That day the Lord exalted(Y) Joshua in the sight of all Israel; and they stood in awe of him all the days of his life, just as they had stood in awe of Moses.

15 Then the Lord said to Joshua, 16 “Command the priests carrying the ark of the covenant law(Z) to come up out of the Jordan.”

17 So Joshua commanded the priests, “Come up out of the Jordan.”

18 And the priests came up out of the river carrying the ark of the covenant of the Lord. No sooner had they set their feet on the dry ground than the waters of the Jordan returned to their place(AA) and ran at flood stage(AB) as before.

19 On the tenth day of the first month the people went up from the Jordan and camped at Gilgal(AC) on the eastern border of Jericho. 20 And Joshua set up at Gilgal the twelve stones(AD) they had taken out of the Jordan. 21 He said to the Israelites, “In the future when your descendants ask their parents, ‘What do these stones mean?’(AE) 22 tell them, ‘Israel crossed the Jordan on dry ground.’(AF) 23 For the Lord your God dried up the Jordan before you until you had crossed over. The Lord your God did to the Jordan what he had done to the Red Sea[b] when he dried it up before us until we had crossed over.(AG) 24 He did this so that all the peoples of the earth might know(AH) that the hand of the Lord is powerful(AI) and so that you might always fear the Lord your God.(AJ)

Footnotes

  1. Joshua 4:9 Or Joshua also set up twelve stones
  2. Joshua 4:23 Or the Sea of Reeds