Zefaniya 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Tsogolo la Yerusalemu
3 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,
owukira ndi odetsedwa!
2 Sumvera aliyense,
sulandira chidzudzulo.
Sumadalira Yehova,
suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,
olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,
zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Aneneri ake ndi odzikuza;
anthu achinyengo.
Ansembe ake amadetsa malo opatulika
ndipo amaphwanya lamulo.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;
Iye salakwa.
Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,
ndipo tsiku lililonse salephera,
komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu;
ndagwetsa malinga awo.
Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,
popanda aliyense wodutsa.
Mizinda yawo yawonongedwa;
palibe aliyense adzatsalemo.
7 Ndinati,
‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa
ndi kumvera kudzudzula kwanga!’
Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,
kapena kuwalanganso.
Koma iwo anali okonzeka
kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova,
“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.
Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,
kusonkhanitsa maufumu
ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;
mkwiyo wanga wonse woopsa.
Dziko lonse lidzatenthedwa
ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse
kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova
ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi
anthu anga ondipembedza, omwazikana,
adzandibweretsera zopereka.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi
chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,
popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu
amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.
Simudzakhalanso odzikuza
mʼphiri langa lopatulika.
12 Koma ndidzasiya pakati panu
anthu ofatsa ndi odzichepetsa,
amene amadalira dzina la Yehova.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;
sadzayankhulanso zonama,
ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.
Adzadya ndi kugona
ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;
fuwula mokweza, iwe Israeli!
Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Yehova wachotsa chilango chako,
wabweza mdani wako.
Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;
sudzaopanso chilichonse.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,
“Usaope, iwe Ziyoni;
usafowoke.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako,
ali ndi mphamvu yopulumutsa.
Adzakondwera kwambiri mwa iwe,
adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,
adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 “Ndidzakuchotserani zowawa
za pa zikondwerero zoyikika;
nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi
onse amene anakuponderezani;
ndidzapulumutsa olumala
ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.
Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu
mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;
pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.
Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu
pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi
pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu
inu mukuona,”
akutero Yehova.
Zephaniah 3
New International Version
Jerusalem
3 Woe to the city of oppressors,(A)
rebellious(B) and defiled!(C)
2 She obeys(D) no one,
she accepts no correction.(E)
She does not trust(F) in the Lord,
she does not draw near(G) to her God.
3 Her officials within her
are roaring lions;(H)
her rulers are evening wolves,(I)
who leave nothing for the morning.(J)
4 Her prophets are unprincipled;
they are treacherous people.(K)
Her priests profane the sanctuary
and do violence to the law.(L)
5 The Lord within her is righteous;(M)
he does no wrong.(N)
Morning by morning(O) he dispenses his justice,
and every new day he does not fail,(P)
yet the unrighteous know no shame.(Q)
Jerusalem Remains Unrepentant
6 “I have destroyed nations;
their strongholds are demolished.
I have left their streets deserted,
with no one passing through.
Their cities are laid waste;(R)
they are deserted and empty.
7 Of Jerusalem I thought,
‘Surely you will fear me
and accept correction!’(S)
Then her place of refuge[a] would not be destroyed,
nor all my punishments come upon[b] her.
But they were still eager
to act corruptly(T) in all they did.
8 Therefore wait(U) for me,”
declares the Lord,
“for the day I will stand up to testify.[c]
I have decided to assemble(V) the nations,(W)
to gather the kingdoms
and to pour out my wrath(X) on them—
all my fierce anger.(Y)
The whole world will be consumed(Z)
by the fire of my jealous anger.
Restoration of Israel’s Remnant
9 “Then I will purify the lips of the peoples,
that all of them may call(AA) on the name of the Lord(AB)
and serve(AC) him shoulder to shoulder.
10 From beyond the rivers of Cush[d](AD)
my worshipers, my scattered people,
will bring me offerings.(AE)
11 On that day you, Jerusalem, will not be put to shame(AF)
for all the wrongs you have done to me,(AG)
because I will remove from you
your arrogant boasters.(AH)
Never again will you be haughty
on my holy hill.(AI)
12 But I will leave within you
the meek(AJ) and humble.
The remnant of Israel
will trust(AK) in the name of the Lord.
13 They(AL) will do no wrong;(AM)
they will tell no lies.(AN)
A deceitful tongue
will not be found in their mouths.(AO)
They will eat and lie down(AP)
and no one will make them afraid.(AQ)”
14 Sing, Daughter Zion;(AR)
shout aloud,(AS) Israel!
Be glad and rejoice(AT) with all your heart,
Daughter Jerusalem!
15 The Lord has taken away your punishment,
he has turned back your enemy.
The Lord, the King of Israel, is with you;(AU)
never again will you fear(AV) any harm.(AW)
16 On that day
they will say to Jerusalem,
“Do not fear, Zion;
do not let your hands hang limp.(AX)
17 The Lord your God is with you,
the Mighty Warrior who saves.(AY)
He will take great delight(AZ) in you;
in his love he will no longer rebuke you,(BA)
but will rejoice over you with singing.”(BB)
18 “I will remove from you
all who mourn over the loss of your appointed festivals,
which is a burden and reproach for you.
19 At that time I will deal
with all who oppressed(BC) you.
I will rescue the lame;
I will gather the exiles.(BD)
I will give them praise(BE) and honor
in every land where they have suffered shame.
20 At that time I will gather you;
at that time I will bring(BF) you home.
I will give you honor(BG) and praise(BH)
among all the peoples of the earth
when I restore your fortunes[e](BI)
before your very eyes,”
says the Lord.
Footnotes
- Zephaniah 3:7 Or her sanctuary
- Zephaniah 3:7 Or all those I appointed over
- Zephaniah 3:8 Septuagint and Syriac; Hebrew will rise up to plunder
- Zephaniah 3:10 That is, the upper Nile region
- Zephaniah 3:20 Or I bring back your captives
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.