Zekariya 13
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kuyeretsedwa ku Tchimo
13 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa. 3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu. 5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’ 6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
Kukantha Mʼbusa, Nkhosa Kubalalika
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga,
ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!”
akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kantha mʼbusa
ndipo nkhosa zidzabalalika,
ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse,
“zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka;
koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto;
ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva
ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide.
Adzayitana pa dzina langa
ndipo Ine ndidzawayankha;
Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’
ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’ ”
Zechariah 13
New International Version
Cleansing From Sin
13 “On that day a fountain(A) will be opened to the house of David and the inhabitants of Jerusalem, to cleanse(B) them from sin and impurity.
2 “On that day, I will banish the names of the idols(C) from the land, and they will be remembered no more,”(D) declares the Lord Almighty. “I will remove both the prophets(E) and the spirit of impurity from the land. 3 And if anyone still prophesies, their father and mother, to whom they were born, will say to them, ‘You must die, because you have told lies(F) in the Lord’s name.’ Then their own parents will stab the one who prophesies.(G)
4 “On that day every prophet will be ashamed(H) of their prophetic vision. They will not put on a prophet’s garment(I) of hair(J) in order to deceive.(K) 5 Each will say, ‘I am not a prophet. I am a farmer; the land has been my livelihood since my youth.[a]’(L) 6 If someone asks, ‘What are these wounds on your body[b]?’ they will answer, ‘The wounds I was given at the house of my friends.’
The Shepherd Struck, the Sheep Scattered
7 “Awake, sword,(M) against my shepherd,(N)
against the man who is close to me!”
declares the Lord Almighty.
“Strike the shepherd,
and the sheep will be scattered,(O)
and I will turn my hand against the little ones.
8 In the whole land,” declares the Lord,
“two-thirds will be struck down and perish;
yet one-third will be left in it.(P)
9 This third I will put into the fire;(Q)
I will refine them like silver(R)
and test them like gold.(S)
They will call(T) on my name(U)
and I will answer(V) them;
I will say, ‘They are my people,’(W)
and they will say, ‘The Lord is our God.(X)’”
Footnotes
- Zechariah 13:5 Or farmer; a man sold me in my youth
- Zechariah 13:6 Or wounds between your hands
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.