Add parallel Print Page Options

Munthu ndi Chingwe Choyezera

Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake. Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?”

Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”

Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka. Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’

“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.

“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!” Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga. Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.

10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova. 11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. 12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu. 13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

A Man With a Measuring Line

[a]Then I looked up, and there before me was a man with a measuring line in his hand. I asked, “Where are you going?”

He answered me, “To measure Jerusalem, to find out how wide and how long it is.”(A)

While the angel who was speaking to me was leaving, another angel came to meet him and said to him: “Run, tell that young man, ‘Jerusalem will be a city without walls(B) because of the great number(C) of people and animals in it.(D) And I myself will be a wall(E) of fire(F) around it,’ declares the Lord, ‘and I will be its glory(G) within.’(H)

“Come! Come! Flee from the land of the north,” declares the Lord, “for I have scattered(I) you to the four winds of heaven,”(J) declares the Lord.(K)

“Come, Zion! Escape,(L) you who live in Daughter Babylon!”(M) For this is what the Lord Almighty says: “After the Glorious One has sent me against the nations that have plundered you—for whoever touches you touches the apple of his eye(N) I will surely raise my hand against them so that their slaves will plunder them.[b](O) Then you will know that the Lord Almighty has sent me.(P)

10 “Shout(Q) and be glad, Daughter Zion.(R) For I am coming,(S) and I will live among you,”(T) declares the Lord.(U) 11 “Many nations will be joined with the Lord in that day and will become my people.(V) I will live among you and you will know that the Lord Almighty has sent me to you.(W) 12 The Lord will inherit(X) Judah(Y) as his portion in the holy land and will again choose(Z) Jerusalem. 13 Be still(AA) before the Lord, all mankind, because he has roused himself from his holy dwelling.(AB)

Footnotes

  1. Zechariah 2:1 In Hebrew texts 2:1-13 is numbered 2:5-17.
  2. Zechariah 2:9 Or says after … eye: “I … plunder them.”