Add parallel Print Page Options

Kuyeretsedwa ku Tchimo

13 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.

“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa. Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.

“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu. Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’ Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’

Kukantha Mʼbusa, Nkhosa Kubalalika

“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga,
    ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!”
    akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kantha mʼbusa
    ndipo nkhosa zidzabalalika,
    ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse,
    “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka;
    koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto;
    ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva
    ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide.
Adzayitana pa dzina langa
    ndipo Ine ndidzawayankha;
Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’
    ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’ ”