Add parallel Print Page Options

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
    amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
    kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
    osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
Iwo anamva njala ndi ludzu,
    ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
    kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
    ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
    amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
    ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
    anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
    ndipo anadula maunyolo awo.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
    ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
    ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
    ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
    anawalanditsa ku manda.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22 Apereke nsembe yachiyamiko
    ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
    Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24 Anaona ntchito za Yehova,
    machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
    imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
    pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
    anali pa mapeto a moyo wawo.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
29 Yehova analetsa namondwe,
    mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata,
    ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
    ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
    akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
    chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
    ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
    ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
    ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
    ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
    chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
    anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
    ngati magulu a nkhosa.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
    koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
    ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

BOOK V

Psalms 107–150

Psalm 107

Give thanks to the Lord,(A) for he is good;(B)
    his love endures forever.

Let the redeemed(C) of the Lord tell their story—
    those he redeemed from the hand of the foe,
those he gathered(D) from the lands,
    from east and west, from north and south.[a]

Some wandered in desert(E) wastelands,
    finding no way to a city(F) where they could settle.
They were hungry(G) and thirsty,(H)
    and their lives ebbed away.
Then they cried out(I) to the Lord in their trouble,
    and he delivered them from their distress.
He led them by a straight way(J)
    to a city(K) where they could settle.
Let them give thanks(L) to the Lord for his unfailing love(M)
    and his wonderful deeds(N) for mankind,
for he satisfies(O) the thirsty
    and fills the hungry with good things.(P)

10 Some sat in darkness,(Q) in utter darkness,
    prisoners suffering(R) in iron chains,(S)
11 because they rebelled(T) against God’s commands
    and despised(U) the plans(V) of the Most High.
12 So he subjected them to bitter labor;
    they stumbled, and there was no one to help.(W)
13 Then they cried to the Lord in their trouble,
    and he saved them(X) from their distress.
14 He brought them out of darkness,(Y) the utter darkness,(Z)
    and broke away their chains.(AA)
15 Let them give thanks(AB) to the Lord for his unfailing love(AC)
    and his wonderful deeds(AD) for mankind,
16 for he breaks down gates of bronze
    and cuts through bars of iron.

17 Some became fools(AE) through their rebellious ways(AF)
    and suffered affliction(AG) because of their iniquities.
18 They loathed all food(AH)
    and drew near the gates of death.(AI)
19 Then they cried(AJ) to the Lord in their trouble,
    and he saved them(AK) from their distress.
20 He sent out his word(AL) and healed them;(AM)
    he rescued(AN) them from the grave.(AO)
21 Let them give thanks(AP) to the Lord for his unfailing love(AQ)
    and his wonderful deeds(AR) for mankind.
22 Let them sacrifice thank offerings(AS)
    and tell of his works(AT) with songs of joy.(AU)

23 Some went out on the sea(AV) in ships;(AW)
    they were merchants on the mighty waters.
24 They saw the works of the Lord,(AX)
    his wonderful deeds in the deep.
25 For he spoke(AY) and stirred up a tempest(AZ)
    that lifted high the waves.(BA)
26 They mounted up to the heavens and went down to the depths;
    in their peril(BB) their courage melted(BC) away.
27 They reeled(BD) and staggered like drunkards;
    they were at their wits’ end.
28 Then they cried(BE) out to the Lord in their trouble,
    and he brought them out of their distress.(BF)
29 He stilled the storm(BG) to a whisper;
    the waves(BH) of the sea[b] were hushed.(BI)
30 They were glad when it grew calm,
    and he guided them(BJ) to their desired haven.
31 Let them give thanks(BK) to the Lord for his unfailing love(BL)
    and his wonderful deeds(BM) for mankind.
32 Let them exalt(BN) him in the assembly(BO) of the people
    and praise him in the council of the elders.

33 He turned rivers into a desert,(BP)
    flowing springs(BQ) into thirsty ground,
34 and fruitful land into a salt waste,(BR)
    because of the wickedness of those who lived there.
35 He turned the desert into pools of water(BS)
    and the parched ground into flowing springs;(BT)
36 there he brought the hungry to live,
    and they founded a city where they could settle.
37 They sowed fields and planted vineyards(BU)
    that yielded a fruitful harvest;
38 he blessed them, and their numbers greatly increased,(BV)
    and he did not let their herds diminish.(BW)

39 Then their numbers decreased,(BX) and they were humbled(BY)
    by oppression, calamity and sorrow;
40 he who pours contempt on nobles(BZ)
    made them wander in a trackless waste.(CA)
41 But he lifted the needy(CB) out of their affliction
    and increased their families like flocks.(CC)
42 The upright see and rejoice,(CD)
    but all the wicked shut their mouths.(CE)

43 Let the one who is wise(CF) heed these things
    and ponder the loving deeds(CG) of the Lord.

Footnotes

  1. Psalm 107:3 Hebrew north and the sea
  2. Psalm 107:29 Dead Sea Scrolls; Masoretic Text / their waves