Add parallel Print Page Options

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

107 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
    amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
    kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
    osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
Iwo anamva njala ndi ludzu,
    ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
    kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
    ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
    amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
    ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
    anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
    ndipo anadula maunyolo awo.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
    ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
    ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
    ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
    anawalanditsa ku manda.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22 Apereke nsembe yachiyamiko
    ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
    Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24 Anaona ntchito za Yehova,
    machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
    imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
    pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
    anali pa mapeto a moyo wawo.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
    ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
29 Yehova analetsa namondwe,
    mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata,
    ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
    ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
    ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
    akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
    chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
    ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
    ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
    ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
    ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
    chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
    anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
    ngati magulu a nkhosa.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
    koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
    ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

Nyimbo. Salimo la Davide.

108 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;
    ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Dzukani, zeze ndi pangwe!
    Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;
    ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;
    kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,
    ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja
    kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
    “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu
    ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
    Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
    Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo
    ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;
    ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?
    Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana
    ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,
    pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,
    ndipo adzapondereza pansi adani athu.

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.

109 Mulungu amene ndimakutamandani,
    musakhale chete,
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo
    atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;
    iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Andizungulira ndi mawu audani,
    amandinena popanda chifukwa.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,
    koma ine ndine munthu wapemphero.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,
    ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.

Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;
    lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,
    ndipo mapemphero ake amutsutse.
Masiku ake akhale owerengeka;
    munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Ana ake akhale amasiye
    ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;
    apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;
    alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima
    kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa,
    mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;
    tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,
    kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.

16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,
    koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka
    ndi osweka mtima.
17 Anakonda kutemberera,
    matembererowo abwerere kwa iye;
sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,
    choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Anavala kutemberera ngati chovala;
    kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,
    kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,
    ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,
    kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.

21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
    muchite nane molingana ndi dzina lanu,
    chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,
    ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,
    ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,
    thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;
    akandiona, amapukusa mitu yawo.

26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;
    pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,
    kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;
    pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,
    koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,
    ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.

30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;
    ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,
    kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

Salimo la Davide.

110 Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,
    “Khala ku dzanja langa lamanja
mpaka nditasandutsa adani ako
    kukhala chopondapo mapazi ako.”

Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;
    udzalamulira pakati pa adani ako.
Ankhondo ako adzakhala odzipereka
    pa tsiku lako la nkhondo.
Atavala chiyero chaulemerero,
    kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,
    udzalandira mame a unyamata wako.

Yehova walumbira
    ndipo sadzasintha maganizo ake:
“Ndiwe wansembe mpaka muyaya
    monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

Ambuye ali kudzanja lako lamanja;
    Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
Adzaweruza anthu a mitundu ina,
    adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;
    choncho adzaweramutsa mutu wake.
111 Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse
    mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

Ntchito za Yehova nʼzazikulu;
    onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,
    ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;
    Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;
    amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
    kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;
    malangizo ake onse ndi odalirika.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,
    ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Iyeyo amawombola anthu ake;
    anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya
    dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;
    onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.
    Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
112 Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,
    amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
    mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
    ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
    wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
    amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

Ndithu sadzagwedezeka;
    munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
    mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
    potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
    chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
    nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
    adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
    Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
113 Tamandani Yehova.

Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
    tamandani dzina la Yehova.
Yehova atamandidwe,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,
    dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,
    ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,
    Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
amene amawerama pansi kuyangʼana
    miyamba ndi dziko lapansi?

Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi
    ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
amawakhazika pamodzi ndi mafumu,
    pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake
    monga mayi wa ana wosangalala.

Tamandani Yehova.
114 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto,
    nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu,
    Israeli anasanduka ufumu wake.

Nyanja inaona ndi kuthawa,
    mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna,
    timapiri ngati ana ankhosa.

Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa?
    iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna,
    inu timapiri, ngati ana ankhosa?

Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi,
    pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime,
    thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
115 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi
    koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,
    chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,
    “Mulungu wawo ali kuti?”
Mulungu wathu ali kumwamba;
    Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,
    opangidwa ndi manja a anthu.
Pakamwa ali napo koma sayankhula,
    maso ali nawo koma sapenya;
makutu ali nawo koma samva,
    mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;
    mapazi ali nawo koma sayenda;
    kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,
    chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.

Inu Aisraeli, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;
    Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:
    adzadalitsa nyumba ya Israeli,
    adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;
    aangʼono ndi aakulu omwe.

14 Yehova akuwonjezereni madalitso;
    inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova,
    Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kumwamba ndi kwa Yehova,
    koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,
    amene amatsikira kuli chete;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Tamandani Yehova.
116 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;
    Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Pakuti ananditchera khutu,
    ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.

Zingwe za imfa zinandizinga,
    zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;
    ndinapeza mavuto ndi chisoni.
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:
    “Inu Yehova, pulumutseni!”

Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama
    Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;
    pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.

Pumula iwe moyo wanga,
    pakuti Yehova wakuchitira zokoma.

Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,
    maso anga ku misozi,
    mapazi anga kuti angapunthwe,
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova
    mʼdziko la anthu amoyo.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,
    “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,
    “Anthu onse ndi abodza.”

12 Ndingamubwezere chiyani Yehova,
    chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso
    ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova
    pamaso pa anthu ake onse.

15 Imfa ya anthu oyera mtima
    ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:
    ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;
    Inu mwamasula maunyolo anga.

17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu
    ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova
    pamaso pa anthu ake onse,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,
    mʼkati mwako iwe Yerusalemu.

Tamandani Yehova.
117 Tamandani Yehova, inu anthu a mitundu yonse;
    mulemekezeni Iye, inu mitundu ya anthu.
Pakuti chikondi chake pa ife ndi chachikulu,
    ndipo kukhulupirika kwa Yehova nʼkosatha.

Tamandani Yehova.
118 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Israeli anene kuti:
    “Chikondi chake ndi chosatha.”
Banja la Aaroni linene kuti,
    “Chikondi chake ndi chosatha.”
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti:
    “Chikondi chake ndi chosatha.”

Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova,
    ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha.
    Munthu angandichite chiyani?
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa.
    Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.

Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova
    kusiyana ndi kudalira munthu.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova
    kusiyana ndi kudalira mafumu.

10 Anthu a mitundu yonse anandizinga,
    koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Anandizinga mbali zonse,
    koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Anandizinga ngati njuchi,
    koma anatha msanga ngati moto wapaminga;
    mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa,
    koma Yehova anandithandiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
    Iye wakhala chipulumutso changa.

15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano
    ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:
“Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16     Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba
    Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo
    ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Yehova wandilanga koopsa,
    koma sanandipereke ku imfa.

19 Tsekulireni zipata zachilungamo,
    kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova
    chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;
    mwakhala chipulumutso changa.

22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana
    wasanduka wapangodya;
23 Yehova ndiye wachita zimenezi
    ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;
    tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

25 Inu Yehova, tipulumutseni;
    Yehova, tipambanitseni.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova.
    Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Yehova ndi Mulungu,
    ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife.
Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu,
    mpaka ku nyanga za guwa.

28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;
    Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.

29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Alefu

119 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
    amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
    amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Sachita cholakwa chilichonse;
    amayenda mʼnjira zake.
Inu mwapereka malangizo
    ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
    pa kumvera zophunzitsa zanu!
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
    poganizira malamulo anu onse.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
    pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
    musanditaye kwathunthu.

Beti

Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
    Akawasamala potsata mawu anu.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
    musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
    kuti ndisakuchimwireni.
12 Mutamandike Inu Yehova;
    phunzitseni malamulo anu.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
    amene amachokera pakamwa panu.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu
    monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Ndimalingalira malangizo anu
    ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu;
    sindidzayiwala konse mawu anu.

Gimeli

17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
    kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
    zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
    musandibisire malamulo anu.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka
    malamulo anu nthawi zonse.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
    amene achoka pa malamulo anu.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
    pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
    mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Malamulo anu amandikondweretsa;
    ndiwo amene amandilangiza.

Daleti

25 Moyo wanga wakangamira fumbi;
    tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
    phunzitseni malamulo anu.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
    pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
    limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
    mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ndasankha njira ya choonadi;
    ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
    musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
    pakuti Inu mwamasula mtima wanga.

He

33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
    ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
    ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
    pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
    osati chuma.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
    sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
    kuti Inu muopedwe.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
    pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
    Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.

Wawi

41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
    chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
    popeza ndimadalira mawu anu.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
    pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
    ku nthawi za nthawi.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu,
    chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
    ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
    chifukwa ndimawakonda.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
    ndipo ndimalingalira malangizo anu.

Zayini

49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
    popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
    lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
    koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
    ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
    amene ataya malamulo anu.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
    kulikonse kumene ndigonako.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
    ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
    ndimasunga malangizo anu.

Heti

57 Yehova, Inu ndiye gawo langa;
    ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
    mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Ndinalingalira za njira zanga
    ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
    kumvera malamulo anu.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
    sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
    chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
    kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
    phunzitseni malamulo anu.

Teti

65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
    molingana ndi mawu anu.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
    pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
    koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
    phunzitseni malamulo anu.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
    ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
    koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
    kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
    kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.

Yodi

73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
    patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
    chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
    ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
    molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
    popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
    koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
    iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
    kuti ndisachititsidwe manyazi.

Kafu

81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
    koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
    Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
    sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
    Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Anthu osalabadira za Mulungu,
    odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika;
    thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
    koma sindinataye malangizo anu.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
    ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.

Lamedi

89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
    akhazikika kumwambako.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
    Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
    pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
    ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
    pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni;
    pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
    koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
    koma malamulo anu alibe malire konse.

Memu

97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
    Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
    popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
    popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
    popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
    kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
    pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
    otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
    kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.

Nuni

105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
    ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
    kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Ndazunzika kwambiri;
    Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
    ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
    sindidzayiwala malamulo anu.
110 Anthu oyipa anditchera msampha,
    koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
    Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
    mpaka kumapeto kwenikweni.

Samekhi

113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
    koma ndimakonda malamulo anu.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
    chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
    kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
    musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
    nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
    pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
    nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
    ndimachita mantha ndi malamulo anu.

Ayini

121 Ndachita zolungama ndi zabwino;
    musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
    musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
    kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
    ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
    kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
    malamulo anu akuswedwa.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
    kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
    ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.

Pe

129 Maumboni anu ndi odabwitsa
    nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
    ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
    kufunafuna malamulo anu.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
    monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
    musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
    kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
    ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
    chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.

Tsade

137 Yehova ndinu wolungama,
    ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
    ndi odalirika ndithu.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
    chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri
    nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
    sindiyiwala malangizo anu.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
    ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera,
    koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
    patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.

Kofu

145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
    ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
    ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
    chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
    kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
    Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
    koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi,
    malamulo anu onse ndi woona.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
    kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.

Reshi

153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
    pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
    sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
    pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
    sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri,
    koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
    popeza samvera mawu anu.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
    sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Mawu anu onse ndi owona;
    malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.

Sini ndi Shini

161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
    koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
    ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
    koma ndimakonda malamulo anu.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
    pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
    ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
    ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Ndimamvera umboni wanu
    pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
    pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.

Tawu

169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
    patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
    pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga,
    pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu,
    popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
    pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
    ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
    ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
    funafunani mtumiki wanu,
    pakuti sindinayiwale malamulo anu.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

120 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,
    ndipo Iye amandiyankha.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,
    ndi kwa anthu achinyengo.

Kodi adzakuchitani chiyani,
    ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,
    ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,
    kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati
    pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Ine ndine munthu wamtendere;
    koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

121 Ndikweza maso anga ku mapiri;
    kodi thandizo langa limachokera kuti?
Thandizo langa limachokera kwa Yehova,
    wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Sadzalola kuti phazi lako literereke;
    Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli
    sadzawodzera kapena kugona.

Yehova ndiye amene amakusunga;
    Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,
    kapena mwezi nthawi ya usiku.

Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;
    adzasunga moyo wako.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

122 Ndinakondwera atandiwuza kuti,
    “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Mapazi athu akuyima mʼzipata
    zako, Iwe Yerusalemu.

Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda
    umene uli wothithikana pamodzi.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,
    mafuko a Yehova,
umboni wa kwa Israeli,
    kuti atamande dzina la Yehova.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,
    mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.

Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:
    “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,
    ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga
    ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,
    ndidzakufunira zabwino.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

123 Ndikweza maso anga kwa Inu,
    kwa Inu amene mumakhala kumwamba.
Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,
    monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,
choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,
    mpaka atichitire chifundo.

Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,
    pakuti tapirira chitonzo chachikulu.
Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,
    chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

124 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
    anene tsono Israeli,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
    potiwukira anthuwo,
iwo atatipsera mtima,
    akanatimeza amoyo;
chigumula chikanatimiza,
    mtsinje ukanatikokolola,
madzi a mkokomo
    akanatikokolola.

Atamandike Yehova,
    amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
    yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
    ndipo ife tapulumuka.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
    wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

125 Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,
    limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu,
    momwemonso Yehova azungulira anthu ake
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala
    pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,
kuti anthu olungamawo
    angachite nawonso zoyipa.

Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,
    amene ndi olungama mtima
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,
    Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

126 Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,
    tinali ngati amene akulota.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;
    malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.
Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,
    “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Yehova watichitira zinthu zazikulu,
    ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,
    monga mitsinje ya ku Negevi.
Iwo amene amafesa akulira,
    adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Iye amene amayendayenda nalira,
    atanyamula mbewu yokafesa,
adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,
    atanyamula mitolo yake.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

127 Yehova akapanda kumanga nyumba,
    omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.
Yehova akapanda kulondera mzinda,
    mlonda akanangolondera pachabe.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa
    ndi kusagona msanga madzulo,
kuvutikira chakudya choti mudye,
    pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,
    ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja
    mwa munthu wankhondo.
Wodala munthu
    amene motengera mivi mwake mwadzaza.
Iwo sadzachititsidwa manyazi
    pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

128 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
    amene amayenda mʼnjira zake.
Udzadya chipatso cha ntchito yako;
    madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
    mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
    kuzungulira tebulo lako.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
    amene amaopa Yehova.

Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
    masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
    ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

129 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
    anene tsono Israeli;
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
    koma sanandipambane.
Anthu otipula analima pa msana panga
    ndipo anapangapo mizere yayitali:
Koma Yehova ndi wolungama;
    Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

Onse amene amadana ndi Ziyoni
    abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
    umene umafota usanakule;
sungadzaze manja a owumweta
    kapena manja a omanga mitolo.
Odutsa pafupi asanene kuti,
    “Dalitso la Yehova lili pa inu;
    tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

130 Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
    Ambuye imvani mawu anga.
Makutu anu akhale tcheru kumva
    kupempha chifundo kwanga.

Inu Yehova, mukanamawerengera machimo,
    Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
Koma kwa Inu kuli chikhululukiro;
    nʼchifukwa chake mumaopedwa.

Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera,
    ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
Moyo wanga umayembekezera Ambuye,
    kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
    inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,

Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
    pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika
    ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
Iye mwini adzawombola Israeli
    ku machimo ake onse.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.

131 Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,
    maso anga siwonyada;
sinditengeteka mtima
    ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
Koma moyo wanga ndawutontholetsa
    ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,
    moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.

Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

132 Inu Yehova, kumbukirani Davide
    ndi mavuto onse anapirira.

Iye analumbira kwa Yehova
    ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga
    kapena kugona pa bedi langa:
sindidzalola kuti maso anga agone,
    kapena zikope zanga ziwodzere,
mpaka nditamupezera malo Yehova,
    malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,
    tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;
    tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,
    Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
Ansembe anu avekedwe chilungamo;
    anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,
    musakane wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira kwa Davide,
    lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:
“Mmodzi wa ana ako
    ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 ngati ana ako azisunga pangano langa
    ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,
pamenepo ana awo adzakhala pa mpando
    wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,
    Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;
    ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;
    anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,
    ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide
    ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi,
    koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

133 Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu
    pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu,
    otsikira ku ndevu,
ku ndevu za Aaroni,
    oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
Zili ngati mame a ku Heremoni
    otsikira pa Phiri la Ziyoni.
Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso,
    ndiwo moyo wamuyaya.

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

134 Bwerani, mutamande Yehova, inu atumiki onse a Yehova,
    amene mumatumikira usiku mʼnyumba ya Yehova.
Kwezani manja anu mʼmalo opatulika
    ndipo mutamande Yehova.

Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,
    akudalitseni kuchokera mʼZiyoni.
135 Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;
    mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,
    mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;
    imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,
    Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,
    kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,
    kumwamba ndi dziko lapansi,
    ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,
    amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula
    ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,
    ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,
    kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu
    ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihoni mfumu ya Aamori,
    Ogi mfumu ya Basani,
    ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,
    cholowa cha anthu ake Aisraeli.

13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,
    mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,
    ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.

15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,
    opangidwa ndi manja a anthu.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula
    maso ali nawo, koma sapenya;
17 makutu ali nawo, koma sakumva
    ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,
    chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.

19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;
    inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;
    Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,
    amene amakhala mu Yerusalemu.

Tamandani Yehova.
136 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino.
Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Yamikani Mulungu wa milungu.
Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Yamikani Ambuye wa ambuye,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.