Add parallel Print Page Options

BUKU LACHIWIRI

Masalimo 42–72

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

42 Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,
    kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.
    Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
Misozi yanga yakhala chakudya changa
    usana ndi usiku,
pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,
    “Mulungu wako ali kuti?”
Zinthu izi ndimazikumbukira
    pamene ndikukhuthula moyo wanga:
momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,
    kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu
ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko
    pakati pa anthu a pa chikondwerero.

Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?
    Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Yembekezera Mulungu,
    pakuti ndidzamulambirabe,
Mpulumutsi wanga ndi     Mulungu wanga.

Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga
    kotero ndidzakumbukira Inu
kuchokera ku dziko la Yorodani,
    ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
Madzi akuya akuyitana madzi akuya
    mu mkokomo wa mathithi anu;
mafunde anu onse obwera mwamphamvu
    andimiza.

Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,
    nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;
    pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.

Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,
    “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
    woponderezedwa ndi mdani?”
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo
    pamene adani anga akundinyoza,
tsiku lonse akunena kuti,
    “Mulungu wako ali kuti?”

11 Bwanji ukumva chisoni,
    iwe mtima wanga?
Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?
    Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,
    Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

BOOK II

Psalms 42–72

Psalm 42[a][b]

For the director of music. A maskil[c] of the Sons of Korah.

As the deer(A) pants for streams of water,(B)
    so my soul pants(C) for you, my God.
My soul thirsts(D) for God, for the living God.(E)
    When can I go(F) and meet with God?
My tears(G) have been my food
    day and night,
while people say to me all day long,
    “Where is your God?”(H)
These things I remember
    as I pour out my soul:(I)
how I used to go to the house of God(J)
    under the protection of the Mighty One[d]
with shouts of joy(K) and praise(L)
    among the festive throng.(M)

Why, my soul, are you downcast?(N)
    Why so disturbed(O) within me?
Put your hope in God,(P)
    for I will yet praise(Q) him,
    my Savior(R) and my God.(S)

My soul is downcast within me;
    therefore I will remember(T) you
from the land of the Jordan,(U)
    the heights of Hermon(V)—from Mount Mizar.
Deep calls to deep(W)
    in the roar of your waterfalls;
all your waves and breakers
    have swept over me.(X)

By day the Lord directs his love,(Y)
    at night(Z) his song(AA) is with me—
    a prayer to the God of my life.(AB)

I say to God my Rock,(AC)
    “Why have you forgotten(AD) me?
Why must I go about mourning,(AE)
    oppressed(AF) by the enemy?”(AG)
10 My bones suffer mortal agony(AH)
    as my foes taunt(AI) me,
saying to me all day long,
    “Where is your God?”(AJ)

11 Why, my soul, are you downcast?
    Why so disturbed within me?
Put your hope in God,
    for I will yet praise him,
    my Savior and my God.(AK)

Footnotes

  1. Psalm 42:1 In many Hebrew manuscripts Psalms 42 and 43 constitute one psalm.
  2. Psalm 42:1 In Hebrew texts 42:1-11 is numbered 42:2-12.
  3. Psalm 42:1 Title: Probably a literary or musical term
  4. Psalm 42:4 See Septuagint and Syriac; the meaning of the Hebrew for this line is uncertain.